25/05/2026
Nkhani ya mtsikana yu ku salima.
Iyeyu ayika lero maliro ake, akuti mtsikanayu anali ndi mimba nde anamuuza kwao achotse yoyamba anachotsa...
Khalekhaleni nkukhalanso ndi ina yachiwiri kuchoka kwa chibwenzi chake chomwechonso, ndipo atamuuza bwenzi lake anamuuza kuti asunge adzalera onse mwana koma makolo ake atanva anamuuza achotsenso chifukwa cha school kuti apitilize, ndipo anamupatsa mankhwala okuti amwe ichoke.
Mimba ija itachoka anali ku chipatala chifukwa chonva ululu wazina zomwe zinatsalira mkati mwake. Atakhala kuchipatala kwa masiku ndithu anatuluka koma anamuuza kuti azikadya za soft kaye chifukwa anali fragile mkati mwake.
Atapita kunyumba chibwenzi chake chija chinamva kuti mimba ija wachotsa ndipo iye sizinamusangalatse nkumuuza kuti chibwenzi chatha.
Iyeyu atanva izi sizinamusangalatse ndipo anamwa paracetamol (Panadol wambiri oposa 20 panthawi imodzi) nkukakhala kutchire yekhayekha, anthu ena mkumuona nkumutengela kuchipatala komwe anakamwalira.
Sad
Kodi olakwa ndindani pankhaniyi?
Makolo?
Chibwenzi?
Or
Iyeyo?